Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 112

Miyambi ya Patsokwe Kuyenda n’kuvina. -Munthu ukakhala kwanu, si bwino kumachitira mwano alendo, chifukwa tsiku lina ukayenda udzawapeza ndipo adzakuchitira zoipanso. Munthu sudziwa kuti mawa ukapezeka kuti. N’zothe- ka kufika kumene sumaganizira kuti ungafikeko. Kuyenda ndi kuseri kwa phazi. -Mawu onena kuti chinthuchi sindichikhulupirira kuti chingachitike, koma chikadzachitika ndidzakhala ndi chim- wemwe kwambiri. Kuyenda usiku si kuona fisi. -Kuyenda usiku ndi kuyenda ndi mdima waukulu, kunja kuli zii ndi zoopsa zosiyanasiyana. Koma si kuti nthawi zonse amene amayenda usiku amakumana ndi afisi. Kuyenda utsi uli tsitu. -Kuyenda ngati munthu wosazindikira. Kuyera ndi madzi a nyemba. -Zinthu zina zimangokongola m’maonekedwe pomwe si zokon- gola kwenikweni. Kuyimba nthungululu pamaliro. -Ngati munthu sukulongosola mbali yako pamlandu, anthu san- gadziwe kuti ndiwe wosalakwa. Umakhala ngati ukuimba nthungululu pamaliro zonse si zimene umafunika kuchita. Ngati anthu akukuimba mlandu, umafunika kulira nkhawa zako zonse. Kuzima chinutu uzimba ukalipo. -Chinutu ndi moto womwe alenje amayatsa pofuna kuvumbulutsa nyama. Nthawi zina ndi bwino kumazimitsa mo- towo chifukwa mawa mudzafunanso kusaka. Tiyenera kumasa- mala ndi zinthu zomwe timagwiritsa ntchito. Komanso, 111