Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 268

Matigari unkaulukira m'mwamba. "Kunja kumachita mdima waukulu kwambiri kukatsala pang'ono kucha," Guthera anatero. "Inde, kwatsaladi pang'ono kucha," Matigari anayankha. "Mwandikumbutsa nyimbo ina yomwe tinkakonda kuimba. Kunjaku kukanachaa, Kunjaku kukanachaa, n'kadapita kukasamba madzi ozizira limodzi ndi mbalame zam'mawa Kunja kwacha tsopano, ndipo dzuwa lawala. Asanamalize kuimba nyimboyo, anamva kulira kwa agalu. "Anthu ena akutitsatira," anatero Matigari. "Koma musaope, konzekani, chifukwa chimenechi ndi chiyambi chabe chamikwingwirima imene tikumane nayo." "Kodi agaluwo akulira kuchokera kuti?" Muriuki anafunsa. "Ali m'chigwa chomwe tadutsa chija," Matigari anatero. Kenako anatsetsereka kuchokera paphiri paja mwakachetechete. M'mbuyo mwawo ankatha kuona matochi a apolisi omwe ankawatsatawo. Matochiwo ankangoyandikirayandikirabe, ndipo posakhalitsa anawayandikira kwambiri. "Ngati titafulumira kwambiri tikhoza kukafika kumene kuli mtengo wamkuyu ndakhala ndikukuuzani uja apolisiwo asanatipeze." anatero Matigari, powalimbikitsa. "Ndikakangovala lamba wanga, palibe wapolisi amene angayerekeze kukawoloka mtsinje, olo atakakhala zikwizikwi." Apolisi aja anawasakasaka usiku wonse. Kenako kunja kunayamba kuwala. Matigari, Guthera ndi Muriuki anali atatheratu. Mtsinje uja sunali kutali, koma kulira kwa agalu 267