Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 22

Matigari chapatali. Wina uja anadzuka n’kukhala pansi akusisita khosi lake ndipo anayang’ana bambo uja moyamikira kwambiri. Koma atangoona kuti bamboyo watenga ndodo, nayenso anadzambatuka n’kuthawa. Bambo uja anangoima panja pa mtaya uja. Atakumbukira kuti tsopano anali atavala lamba wamtendere, anaponyera pansi ndodo ija ndipo anayamba kutsatira ana aja. Pamene ankawatsatira, anaona apolisi anali ndi galu aja, woyendetsa chigalimoto cha zinyalala chija komanso azibambo ankatolera ndalama kwa ana aja atapanga kamsonkhano kawo pakatchire kanali pambali pamsewu uja. Anaima moyandikana kwambiri ndipo pankamveka phokoso la kuwerengera ndalama zasiliva. Bamboyo anadziyankhulira yekha kuti, “Zoona anthuwa akugawana ndalama zomwe alandira kuchokera kwa anawa? Kodi zikuchitikabe kuti anthu ochepa azipindula chifukwa cha kuzunzika kwa anthu ambiri? Zoona khama komanso ntchito yakalavulagaga ya anthu ambiri izipindulitsa anthu ochepa? Ndi mafunso ngati omwewa omwe anachititsa kuti azikakhala moyo wothawathawa m’mapiri komanso kunkhalango kuja. Koma limenelo linali kale. Iye anadzifunsa kuti, “Nanga n’chifukwa chiyani zinthuzi zikuchitikabe masiku ano popeza tinalandira ufulu wathu?” Kenako anakumbukiranso nyumba yake. Iye anali asanafikeko. Apa njala yokaona kunyumba kwake ija inamubwereranso ndipo inangokhala ngati yagwirizana ndi ludzu komanso malikhweru omwe ankalira kumimba kwake komwe kunakhala pululu kwa masiku ambiri. 21