Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 206

Matigari Gawo 2 Nkhaniyo inadziwika koyamba cha m'ma 10 koloko m'mawa ndipo inalengezedwa pa Wailesi ya Choonadi. Inanena kuti an- thu openga angapo athawa kuchokera kuchipatala cha anthu amisala. Sizinkadziwika kuti athawa bwanji, koma apolisi ankaganiza kuti n'kutheka anagwiritsa ntchito macheka podula waya yemwe anazungulira chipatalacho. Koma oyang'anira chipatalachi anadabwa kwambiri kuti od- walawo anapeza bwanji machekawo chifukwa zinthu zonse monga mitengo, malezala kapena chilichonse chakuthwa sichinkaloledwa kulowa m'chipatalacho. Komanso ngakhale od- walawo ankawadula zikhadaba. Ankachita zimenezi kuti od- walawo asakhadzule anzawo milomo kapena kuwalemba nazo anzawo kumaso. Apolisi anapitiriza kufufuza nkhaniyi, ndipo inalengezedwa pawailesi. Boma linachenjeza anthu kuti akhale osamala, chifu- kwa ankaona kuti amisalawo ayenera ali ndi zida zomwe an- gavulaze nazo anthu. Komanso aliyense analimbikitsidwa kuti azimvetsera wailesi chifukwa aposili apitirizabe kupereka malipoti a mmene nkhani- yo ikuyendera. Ananena kuti wailesi iwauza amisalawo akag- widwa. 205