Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 169
Matigari
“Munthu amene watsala kuti timugwire ndi amene
akumadzitchula kuti Matigari ma Njiruungi. Koma ndikufuna
kumuchenjeza munthu ameneyu. Dzanja la lamulo ndi lalitali
kwambiri kuposa nsewu womwe wasankha keyendawu. Basi
nkhani yamphekesera yabodzayi yathera pamenepa, ndipo is-
amvekenso m’midza yonse ya kuno. Kunkhalango kulibenso
anthu omenyera ufulu wadziko lino. Iwo anabwerera kalekale
pamene tinalandira ufulu wathu n’kukweza mbendera yadziko
lathu. Anthu amene anakana kubwerera, onse anawom-
beredwa, full sto p*. Amene ali ndi makutu amve. Ndipo amene
alibe akabwereke a mayi ake!”
*Amenewa ndi mawu achingelezi omwe amanenedwa potsindika kuti palibenso
zina zowonjezera. Zomwe zanenedwazo n’zokwanira.
“Tsopano tiyeni tibwere kunkhani imene yandibweretsa
kuno: Nkhani ya kusamvana pakati pa ogwira ntchito komanso
oyendetsa fakitale ya Leather and Plastics. Ndisanapite patali,
ndinauzidwa kuti pakhala kamwambo kenakake kapadera . . . ”
Nthawi yomweyo Robert Williams komanso John Boy anad-
zuka. Robert Williams anapereka cheke komanso mapepala
enaake kwa John Boy. Nayenso John boy anapereka zinthuzo
kwa nduna ija. Kenako anakhala pansi.
“Choyamba ndiyamikire oyendetsa kampaniyi chifukwa cha
ntchito yotamandika imene agwira. Mwachiona cheke ichi?
Tachiyang’anani bwinobwino. Ife timafuna kumachita zinthu
zonse poyera. Lino ndi dziko lachikhristu komanso timatsatira
mfundo za demokalase ndipo timachita zonse moona mtima.
Ichi ndi cheke cha 50,000 shillings ndipo chaperekedwa ku-
thumba la apulezidenti lothandiza ana olumala. Kampani imen-
eyi ili ndi anthu amtima wachifundo, achikondi komanso
owolowa manja! Tathokoza kwambiri chifukwa cha zimene
168