Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 101

Matigari M’mapolisi onse a m’tauni muno munadzadza. Anthu ena omwe tinagwidwira limodzi awatsekera kupolisi ina, koma kungoti ku- meneko malo anatha, n’chifukwa chake anandibweretsa kuno. N’chifukwatu ndinakufunsani kuti: Kodi ndinudi Matigari ma Njiruungi?” “Inde, monga mmene wanenera, ndine amene,” Matigari anayankha. Kenako anafunsa wogwira ntchitoyo, “Kodi ukudzi- wa ngati Ngaruro wa Kiriro wamangidwa?” “Sindikudziwa, koma ndamva apolisi akunena kuti akumu- fufuza paliponse. Zikuoneka kuti anakwanitsa kuwazemba,” wogwira ntchito uja anayankha. “Kodi chilungamo chabisala pati m’dziko muno?” Matigari anafunsa akukumbukira Ngaruro wa Kiriro komanso mmene anamuthandizira masana a tsikulo. “Ndiyankha funso limene mwafunsali,” munthu anaba nsima uja anatero. “Musaganize kuti ndikukupeputsani kapena ku- kuonerani m’botolo. Ndikufuna ndikuuzeni kuti mukapitiriza kufunsa mafunso mukufunsawa, akupititsani kuchipatala cha amisala kapena akakuponyerani m’dzenje lamdima wandiwey- ani.” “Dzenje lakuya kuposa limene tatsekeredwali?” wamowa uja anafunsa. Kenako anatembenukira kwa Matigari. “Kuyambira lero uzidziwika kuti Wofunafuna Choonadi ndi Chilungamo. Mtima pansi! Mwana wa Mulungu anabatizidwa ndi Yohane M’batizi. N’chifukwa chake ndatenga udindo wokubatizani inuyo.” “Choonadi kufunafuna Chilungamo?” Mlimi uja anananena chapansipansi podabwa ndi zimene wamowa uja ananena. “Chilungamo kufunafuna choonadi? Wofunafuna Choonadi ndi Chilungamo!” 100