Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 67

Paphata pa Chichewa sanadye nsima koma angodya zina. Chitsanzo: Sitinadye, tangogonera mabanzi. Gonera pamphumi: Kuchita zinthu mochedwa. Chitsanzo: Ife tagonera pamphumi osadziwa kuti anzathu akukatamuka ndi bizinezi ya nsomba. Gontha m’kutu: Kusamva. Chitsanzo: Munthu akamafuna kufa amayamba n’kugontha m’kutu. Gontham’kutu: Munthu wosamva. Tanthauzo lenileni la dzinali ndi tizilombo touluka tofanana ndi ngumbi tomwe timakhala tocheperapo. Chitsanzo: Amene uja ndi gontham’kutu. Gonthi: Munthu wosamvera. Mawuwa amatanthauzanso munthu amene saamva mwachibadwa kapena chifukwa cha matenda. Koma ndi oletsedwa ndi mabungwe oona za ufulu kwa anthu olumala. Chitsanzo: Mwanayu ndi gonthi. Gudu: Munthu wolowerera za eni asanamvetse nkhani yonse. Chitsanzo: Inutu ndi gudu wogudukira zinthu za eni. Mwamva kuti nkhaniyitu ikukukhudzani? Gulidwa: Kuchitira munthu chinachake chifukwa wakugwiritsa kenakake. Chitsanzo: Apolisi ambiri amakhotetsa mlandu akagulidwa. (2) Kodi wosewera ameneyu amugula eti, n’chifukwa chiyani wadzichinya yekha? Gulula mano: Menya modetsa nkhawa. 66