Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 61
Paphata pa Chichewa
amfumu anawafula (anafulidwa).
(b) Kuchotsa malesa a njuchi.
Chitsanzo: Tikukafula uchi.
(c) Kuunjika dothi kapena mchenga.
Chitsanzo: Nkhululu zafula.
Fulatira:
(a) Kusiya kuyang’ana munthu mwadala.
Chitsanzo: Nditawayang’ana, anandifulatira.
(b) Kukunyanyala.
Chitsanzo: Mulungu watifulatira.
Fumbatitsa:
(a) Kupatsa munthu ndalama.
Chitsanzo: Ukagwira ntchitoyi ndikufumbatitsa kenakake.
(b) Kugwiritsa chinachake m’manja.
Chitsanzo: Kodi akufumbatitsa chiyani, ndalama?
Fumbi lokhalokha: Anthu ambirimbiri.
Chitsanzo: Kumaliroko kunali fumbi lokhalokha.
Fumbi ndiwemwini: Mawuwa amatanthauza kuti nthawi
zina ndi bwino kumanena zabwino zokhudza iwe mwini
kuti zikuyendere. Angatanthauzenso kuti ngati ukufuna
zikuyendere umafunika kulimbikira wekha.
Chitsanzo: Ndinadziwa kuti akokomeza kwambiri
zokhudza zimene amadziwa, paja fumbi ndiwemwini.
Fumbi: Anthu ambiri, zinthu zambiri.
Chitsanzo: Anthu omwe amawatsatira anali fumbi.
Fumbwa:
(a) Kudikira nthawi yaitali, kuchedwa.
Chitsanzo: Anatidikiriritsa ife mpaka kufumbwa.
60