Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 367

Paphata pa Chichewa ndikuundwa pano. (2) Inutu muundwira pamzere pano! Ung’onoung’ono: Zovala zothina zomwe zimasokedwa ngati ulusi unawathewa. Chitsanzo: Mnyamata asamavale ngati nkhalamba, ayenera kumaphinza ung’onoung’ono! Ungwiro: Kukhala munthu wosachimwa, kusalakwitsa chilichonse. Chitsanzo: Mkazi wangwiro ndani angam’peze? Unikira: Thandiza munthu kuyambanso kuona bwino zinthu, thandiza munthu wina nzeru. Chitsanzo: Sindinabwere kudzakuuzani zochita, ndimangofuna ndikuunikireni. Unjirira: (a) Kuzunguliridwa ndi anthu. Chitsanzo: Anthu angomuunjirira. (b) Kutolera zinyalala. Chitsanzo: Amene saunjirira saotha nawo. Unjiunji: Kubwera anthu ambiri nthawi imodzi, kuunjika- na. Chitsanzo: N’chifukwa chiyani anthu angoti unjiunji? Unthama: Kunama. Chitsanzo: Ine ndinkadziwa kuti akuunthama. Unyinji: Anthu ambiri. Chitsanzo: Kumowako kunali unyinji. Unyizi: Ulesi. Chitsanzo: Mwanayu ali ndi unyizi. Unyizi: Ulesi. Chitsanzo: Mwanayu ndi waunyizi. Unyolo: Chipangizo chachitsulo chomwe apolisi amamangira opalamula. Chitsanzo: Anamukwidzinga ndi unyolo. 366