Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 365

Paphata pa Chichewa Ukadyole: Woneneza ena kuti iyeyo akome. Chitsanzo: Anthu ena amapita kwa amfumu n’kukachita ukadyole kuti akome. Ukamira mankhwala: Anthu ena omwe akudwala amawiritsa mankhwala n’kutenga nsalu n’kudzifunditsa nawo atayang’ana mankhwala owira aja mpaka atachita thukuta. Chitsanzo: Uukamire mankhwalawa ngati ukufuna ku- chira. Ukhalira zomwezo: Mawuwa amanenedwa munthu akakhumudwa ndi zimene wina akunena. Nthawi zambiri zimene winayo amachita zimakhala zoti n’zosathandiza. Chitsanzo: Ukhalira zomwezo! Anzako akulimbikira ntchi- to n’kumathandiza mabanja awo. Ukufuna ndichite kukuvulira kuti ukhulupirire? Mawu- wa amagwira ntchito munthu wina akamakaikira akuona umboni womveka bwino. Angatanthauze ukufuna ndichite chiyani kuti ukhulupirire? Chitsanzo: Iwe ndi Thomasi Didimo, ukufuna ndichite ku- kuvulira kuti ukhulupirire? Ukumu: Mphamvu. Chitsanzo: Ife tilibe ukumu wochita zimenezi. Ulalo: Mlatho. Chitsanzo: (1) Amene safuna kunyowa akadutse paulalo. (2) Muzidutsa paulalo mungadzapite ndi madzi. Ulaya: Europe. Chitsanzo: Apira ku Ulaya. Ulemu wogwada mgolosale: Ulemu wonyanyira, ulemu wosaona malo. Chitsanzo: Mwanayu ali ndi ulemu wogwada m’golosale. Ulova: Kusowa ntchito yoti uzigwira makamaka yolem- bedwa. Munthuyo amatchedwa lova. Chitsanzo: Anawachotsa ntchito moti panopa ali paulova. 364