Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 362

Paphata pa Chichewa Tsumba: (a) Manyazi. Chitsanzo: Mayiyo anadzuka pamalowo tsumba lili njo. (b) Kumeta m’malimbu n’kusiya tsitsi pakati pa mutu chakutsogolo. Chitsanzo: Wametetsa tsumba. Tswanya: (a) Kuphwanya, kuswa, kunyenya. Chitsanzo: Ndinamupempha kuti anditswanyire mtedza. (b) Kumenya koopsa. Chitsanzo: Anzake amutswanya koopsa. (c) Kuvulaza. Chitsanzo: Mwala wanditswanya. Tukula khutu: (a) Ulula pang’ono. Chitsanzo: Ndikanadziwa kuti akupita kumudzi ndikanamutukula khutu. (b) Kumvetsera mwatcheru. Chitsanzo: Aliyense watukula makutu kuti amve zimene tikukambirana. Tukumuka: Kudzikweza, kudzimva. Chitsanzo: Ndinadziwa kuti ayamba kutukumuka. Tukwanitsa: Wolongolola, mwana kapena munthu wochititsa kuti ena azikunena. Chitsanzo: Mwana uyu ndi wotukwanitsa, taonani ali manja lende. Tula nkhawa: Uza munthu wina mavuto ako kuti akuthandize. Chitsanzo: Ndikupita kukawatulira nkhawa zanga. Tulira nkhwinya: Kubwezera cholakwa kwa wosalakwa. Chitsanzo: Angokutulirani nkhwinya, ndinu wosalakwa. 361