Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 348

Paphata pa Chichewa Taya msuzi: Kutaya mbiri yabwino. Chitsanzo: Ukalephera kudzigwira umatha kuchita zosay- enera ndipo umataya msuzi wonse. Tayale: Zili bwino. Chitsanzo: Zithu zonse zili tayale. Tayana: Lekana, dana. Chitsanzo: Anthu ankagwirizana aja anatayana. Tchaina: Chosalimba. Chilichonse masiku ano ndi cha tchaina. Tchaye: Tiyi. Chitsanzo: Apita kukamtini kukamwa tchaye. Tchemba: Chitini kapena chinthu chimene anthu amakodzeramo usiku akamaopa kutuluka panja. Chitsanzo: Lero sanatulutse tchemba wake. Tchera kumwezi: Kulephera, kutulukiridwa kuti umana- ma. Mawuwa amanenedwa ukazindikira kuti munthu amafuna kukupusitsa, ndiye wamutulukira. Chitsanzo: Amaganiza kuti akadzimvetsa chisoni ndi- wapatsa ndalama, atchera kumwezi. Tchera: Kukukonzera chiwembu, kufuna kukukola. Chitsanzo: Akufuna kunditchera kuti wolakwa ndikhale ine. Tchika: Bedi, chitanda, kama. Chitsanzo: Wodwalayo anamuika patchika. Tchimo: Kuchita zinthu zoipa. Chitsanzo: Munthuyu wachita tchimo. Tchingo: Mpanda. Chitsanzo: Akumanga tchingo kuti tisamapiteko. Tchipa: (a) Kumangolola aliyense. Chitsanzo: Atsikana ovuta uja anatchipa masiku ano. 347