Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 333

Paphata pa Chichewa Puma mwakathithi: Kumuma mwamphamvu, mosale- keza. Chitsanzo: Anatipeza akupuma mwakathithi, mwina zilipo zoopsa zimene anaona, apo ayi ndiye kuti amamuthaman- gitsa. Pumitsa mapazi: Kusiya kuyenda wapansi, kuyenda pa- galimoto kapena njinga. Chitsanzo: Ndagula njinga kuti ndipumitseko mapazi. Punduka: Wopuwala, yemwe ali ndi chiwalo chomwe chili ndi vuto, mwina kupindika kapena kuduka. Mawuwa ndi oletsedwa ndi mabungwe oona za ufulu wa anthu. Chitsanzo: Ndikumenyera ufulu wa anthu opunduka. Punzipunzi: Kudzilimbitsa kuti usagwe ukamamenyedwa kapena ukamayenda modzikoka. Chitsanzo: Ndinawaona ali punzipunzi kulowera kumsika. Puta tsoka: Kudzibweretsera tsoka kapena mavuto. Chitsanzo: Zoona angatukwane munthu wosalakwa uja, kuliputatu tsoka kumeneko! Puta: Palamula, kuyambana ndi munthu wina. Chitsanzo: Wandiputa dala, ndimutibula. (2) Akandiputanso ndimumenya. Putira nkhondo: Kuika wina m’mavuto. Chitsanzo: Ana anga mwandiputira nkhondo, bwanji osakhuzumukako inu! Puwaniza: Kuphwanya. Chitsanzo: Apuwanizapuwaniza mango aja. Puya madyedwe: Kudya zambiri kuposa mnzako. Chitsanzo: Tikamapanga bulitsa, anthu ena amayambitsa nkhani kuti awapuye anzawo madyedwe. Pwamwantha: Menya modetsa nkhawa. Chitsanzo: Munthu woyerekedwa uja anamupwamwantha anzake. 332