Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 322

Paphata pa Chichewa Patelera: Pavuta. Chitsanzo: Ataona kuti patelera, anangochokapo. Pathala: Kusamba kwa akazi. Chitsanzo: Palibe mkazi amene sakhala pathala. Pathupi: Mayi amene watenga mimba, mayi wa pakati. Chitsanzo: Akazi awo ali ndi pathupi. Patsemtedzaupaone (ponyamtedzaupaone): Munthu wandevu zambiri pakamwa komanso pachibwano pake. Chitsanzo: Ndinakumana nawo dzulo. Bambo aketu ndi a patsemtedzaupaone. Patukana: Kusiya kukhalira limodzi kwa anthu omwe anali pabanja. Chitsanzo: Anthu akwatirana dzana aja apatukana. Payera: Zatha. Chitsanzo: Ndimafuna kukathyola misale, koma nditafika ndinapeza payera. Paza: Kungodutsa, kungoyenda. Chitsanzo: Sindinabwere kudzakhazikika, ndikungopaza. Pazamwala: Tambwali. Chitsanzo: Aliyense amadziwa kuti amene uja ndi pa- zamwala, palibe angamukongoze ndalama. Pendapenda: Kusayenda bwino kwa zinthu. Mawuwa amatanthauzanso kuyenda ngati ukufuna kugwa. Chitsanzo: (1) Pakatipa zinthu zinali pendapenda. (2) Pen- dapenda si kugwa koma kuchalira ulendo. Penyera m’madzi: Yang’ana monyoza. Chitsanzo: Anthu aja ayamba kupenyerana m’madzi. Penyera patali: Kukhala ngati sakukuona. Chitsanzo: Titafika kumudzi, sanabwere kudzatipatsa moni moti amangotipenyera patali. Penyerana m’kodi: Kudana. Chitsanzo: Anyamata aja akupenyerana m’kodi. 321