Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 319
Paphata pa Chichewa
Pakona: Pamavuto, zisakuyenda.
Chitsanzo: Nthawi zambiri mwayi ngati umenewu uman-
dipeza ndili pakona.
Pakula ndalama: Kuba ndalama zambiri.
Chitsanzo: Anthu ena a m’boma amapakula ndalama.
Pala mano: Chenjeretsa.
Chitsanzo: Ukapusa naye munthu ameneyu akupala
mano.
Pala moto kudambwe: Palamula.
Chitsanzo: Pamenepatu wapala moto kudambwe.
Palana ubwenzi: Kukhala paubwenzi, kugwirizana.
Chitsanzo: Akufuna tipalane nawo ubwenzi.
Palanga: Pala ndi mpeni ngati nyama yankhumba.
Chitsanzo: Akupalanga nyama kuseriku.
Palasika: Kalipira, kupsa mtima.
Chitsanzo: Atamva zoti mwana wawo walephera mayeso,
anayamba kupalasika.
Palasira makala a moto: Kuika m’mavuto.
Chitsanzo: Anthu oipa mtima ngati awa amakonda
kupalasira anzawo makala a moto.
Pali wina angati fwee apa! Pali wina angachite makani,
pali wina anganditsutse.
Chitsanzo: Ngati pali wina amene angati fwee abwere apa!
Paliwombo: Pakati kapena pamwamba pa mutu.
Chitsanzo: Mwanayu sanakhwime paliwombo.
Pam’konda: Mvula yogwa mbali imodzi.
Chitsanzo: Anadzikodzera poganiza kuti anyowabe ndi
mvulayo. Koma anachita manyazi chifukwa mvula ya
pamkondayo inangodutsa umo, n’kukata.
Pamchenga: Kuphweka, kukhala chosavuta.
Chitsanzo: (1) Timu imeneyi ndi pamchenga. (2) Mayeso
ake anali pamchenga.
318