Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 306

Paphata pa Chichewa Nthyole: Chikwapu. Chitsanso: Mwana wamwano amakhala bwenzi la nthyole. Ntibu: Wailesi. Chitsanzo: Agula ntibu. Ntolo: Mavuto, mulu womangidwa pamodzi wa nkhuni. Chitsanzo: (1) Ndani angatitule ntolowu! (2) Wasenza ntolo wankhuni. Ntopola: Mwano, zachipongwe. Chitsanzo: Akapitirizabe kuchita zantopola amenyedwa. Nunkha chitonde: Kununkha thukuta ngati mmene mbuzi yaimuna imachitira. Zimakonda kuchitikira amu- na. Chitsanzo: Nditalikire, ukununkha chitonde! Nyala: (1) Kuchita manyazi. Chitsanzo: Namwali ayenera kunyala akakumana ndi mwamuna. (b) Kudikira nthawi yaitali. Chitsanzo: Mudikirira mpaka kunyala. Nyambita mapazi a munthu: Nyengerera. Chitsanzo: (1) Kuteroko anabweranso kudzakunyambitani mapazi. (2) Kuti andithandiza akufuna ndichite kuwan- yambita mapazi. Nyambita mwana (munthu): Kulekerera mwana, kulera mwana momunyengerera. Chitsanzo: Anakula mopulukira chifukwa makolo awo ankawanyambita. Nyambitana: Kukondana kwambiri. Chitsanzo: Banja limene lija limachita kunyamitana. Nyambo m’masiku: Lidzafika tsiku lake. Chitsanzo: Asiyeni, nyambo m’masiku. Adzatifuna! 305