Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 303
Paphata pa Chichewa
yolimba ngati imeneyi. (2) Anazolowera kugwira ntchito
yolimba.
Ntchito yowawa (ntchito yopweteka): Ntchito yomwe
susangalala kuigwira chifukwa umavutika nayo kapena
ndi yofuna mphamvu kwambiri.
Chitsanzo: Amagwira ntchito yowawa tsiku lonse.
Ntchona: Munthu yemwe anachoka kwawo n’kukakhazi-
kika kwinakwake. Nthawi zinanso angatanthauze munthu
amene amachita zautambwali.
Chitsanzo: Ameneyu ndi ntchona ya m’tauni muno.
Nthabwala:
(a) Nkhani zoseketsa anthu.
Chitsanzo: Achimwene anu ndi a nthabwala.
(b) Wokonda zoseka.
Chitsanzo: Amalume ndi anthabwala.
Nthabwala: Wokonda kukamba nkhani zoseketsa.
Chitsanzo: (1) Bambowa ndi anthabwala. (2)
Ndinamupeza akunena nthabwala.
Nthambo:
(a) Chingwe kapena waya wantali.
Chitsanzo: Ndani wamangirira nthambo yake apa?
(b) Mwado, panti.
Chitsanzo: Zoona mungayanike nthambo zanu pachingwe?
Nthanda: Munthu wokongola kwambiri.
Chitsanzo: Achiredzerere aja anakwatira kanthanda ka
pantundapo.
Nthata: Wokakamira.
Chitsanzo: Mnyamata ameneyu ndi nthata eti, monse
ndayambira kumukana muja!
Nthawi yabwino: Nthawi yoyenera kuchita zinthu, nthawi
yopanda mavuto.
Chitsanzo: Imeneyi ndi nthawi yabwino yoyamba kulima.
302