Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 300

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Anamalira onse anamanga nsangamutu. Nsanje: (a) Mtima wosafuna kuti wina zizimuyendera. Chitsanzo: Munthu ameneyu amandichitira nsanje. (b) Kusafuna kuti munthu wina azicheza ndi mwamuna kapena mkazi wako. Chitsanzo: Atelala mundilinge ndi maso, amunanga nsanje! Nsanza zokhazokha: Usiwa. Chitsanzo: Mukuseweretsa ndalama apa, chonsecho ma- kolo anu ali nsanza zokhazokha. Nsapule: Ndolo zovala m’makutu. Chitsanzo: Nduke zenizeni zimatchena nsapule. Nsasa: Kanyumba komangidwa ndi udzu. Nthawi zina an- thu amanena dzinali akamatchula nyumba yawo kapena kumene amakhala. Chitsanzo: (1) Amanga misasa yoti achitireko chinamwali. (2) Kameneka ndiye kansasa kathu. Nsatsi: Mafuta ochokera ku zitsamba zinazake. Chitsanzo: Kale anthu ankadzola mafuta a nsatsi. Nseko: Kasekedwe, kuseka. Chitsanzo: (1) Ndinadziwa kuti nseko umenewo ndi wa achimwene. (2) Amakamba nkhani zokodola nseko. Nsengwa: Lichero, lisero, thunga. Chitsanzo: Mubweretse kansengwa kuti titengeromo masamba. Nsenye: Mwana wongobadwa n’kupitirira. Chitsanzo: Munthu yemwe sakhutitsidwa ndi zimene ali nazo amaposedwa ndi nsenye. Nsima tepetepe (teputepu): Nsima yosalimba. Chitsanzo: N’chifukwa chiyani waphikanso nsima ya tepetepe (teputepu). 299