Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 274

Paphata pa Chichewa Munthu wowola m’kamwa: Wotukwana. Chitsanzo: Sitifuna anthu owola m’kamwa, angationongere ana pakhomo pano. Munye kupala champhongo: Wamng’ono woposa wamkulu, monga ana ang’onoang’ono ali ndi ana, pomwe akulu alibe. Chitsanzo: Nthumbidwa zonse timazinyamula pamiyendozi, zasanduka makolo. Ndithu munye kupala champhongo. Muphulika maso: Muona zosaona. Chitsanzo: Usayang’ane ungaphulike maso. Musandipomboneze: Musandisokoneze. Chitsanzo: Musandipomboneze inu, mukuti wapita kumsika pomwe ndakumana naye kuseliku? Mutu umodzi: Munthu m’modzi, wekhawekha. Chitsanzo: (1) Mutu umodzi sungalimbane ndi mavuto amenewa. (2) Vuto limeneli likufuna anthu angapo, osati mutu umodzi. Mutu wa banja: Mwamuna. Chitsanzo: Mutu wa banja ndi amene ayenera kupezera ana zosowa za pamoyo wawo. Mutu wake umakoka: Mutu wake umagwira. Chitsanzo: Mwanayu mutu wake umakoka. Mutu wandikula kapena wandilemera: Kusowa chochita. Chitsanzo: Vutoli lakula ndipo mutu wandilemera (wandikula). Mutu: Mowa woyamba kutchezedwa. Chitsanzo: Ndinadziwa zoti mayi amene aja aukazinga nditalawa mutu wa kachaso yemwe anatcheza dzulo. Muyeso (muyezo): Choyezera. Chitsanzo: Muyeso uli kuti? 273