Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 272

Paphata pa Chichewa Mudzi: (a) Manda, nthumbira. Chitsanzo: Mupite ndi awa akakulozereni mudzi umene achimwene anu anagona. (b) Matenda otupa maliseche, ena amati mdidi. Matenda- wa amakonda kugwira amuna. Chitsanzo: Akuvutika ndi mudzi. Mudzi: Manda Chitsanzo: Adzukulu atamaliza kukumba mudzi woti aike malirowo, anangoona kwatulikira chinjoka, moti onse analikumba liwiro. Muisova: Popeza mwadziwa izizi, muona zimene mungachite. Mawuwa anachokera kuchingerezi. Chitsanzo: Popeza mwamva, muisova. Mukadayenda: Mukadali ndi moyo. Chitsanzo: (1) Ndi bwino mukonze tsogolo la ana anu mukadayenda. (2) Ndinali munthu ine agogo akadayenda. Mulu: Zinthu zounjikana. Chitsanzo: (1) Ali ndi mulu wa ndalama. (2) Ndani waun- jika mulu wamanyiwu? Mumphipi: M’mbali. Chitsanzo: Akufuna matabwa a mphipi zazikulu. Mumpoto mosapita therere: Amangodyera nyama, sa- konda masamba. Chitsanzo: Mayiwa ndi a dovu, mpoto mwake simupita the- rere. Munali kale: Zinkakuyenderani kale, munatha inu. Chitsanzo: Munali kale inu, ndalama zikukuyanjani. Munasamba pati? Mawuwa amatanthauza kuti chinsinsi chanu ndi chani? Chitsanzo: Munasamba pati anzathu kuti zizikuyenderani chonchi? 271