Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 265

Paphata pa Chichewa Mphitapansi: Wochita chiwembu mobisalira. Chitsanzo: Simumadziwa kuti amene uja ndi mphitapansi? Mphulupulu: Kusamvera, kuvuta. Chitsanzo: Mwana wanuyu ndi wamphulupulu. Mphumi: Mwayi. Chitsanzo: Amene achita mphumi ndi a Nasimango. Mphungusatayanthenga: Munthu womana kwambiri kapena woumira. Mphungu ndi mbalame yomwe imauluka m’mwamba kwambiri ndipo nthenga yake ikathothoka, imaiwakha isanafike pansi. Chitsanzo: (1) Zakudya zawotu amadyera mugombeza. Amene aja ndi mphungusatayanthenga. (2) Mwanuna wawo ndi phungusatayamthenga. Mphuno bii: Mawu achipongwe onena za munthu yemwe simukufuna mutamuona. Chitsanzo: Tamuonani, ali mphuno bii, kaya wabwera kudzatani? Mphuno zipida: Pang’ono kwambiri. Chitsanzo: Ndinamutuma kuti akatenge zonse, koma anangonditengera mphuno zipida. Mphuno: Kakang’ono. Chitsanzo: Ndinamutuma kuti akatenge zonse, koma anangonditengera mphuno. Mphwanga: Mng’ono wanga. Chitsanzo: Uyu ndi mphwanga. Mphwayitolo: Waulesi, munthu womati chioneke chion- eke. Chitsanzo: Kukacha koma kuothera dzuwa, mukamuuza kuti akalime amanamizira kudwala. Amene uja ndi mphwayitolo. Mphwephwa: (a) Munthu wopanda mphamvu. 264