Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 249

Paphata pa Chichewa kumeneko, mbuzi ikakonda, amalonda ali pafupi. Mbuzi: Mawuwa amanena za munthu wosamva. Angatan- thauzenso chiweto cha mbuzi. Chitsanzo: (1) Mwana uyu ndi mbuzi! (2) Pamalilowo ma- fumu ambiri anapereka mbuzi. Yemwe amalengeza zime- nezi atatopa kunena kuti amfumu akutiakuti apereka mbuzi, anayamba kumangonena kuti amfumu akuti, mbuzi. Amfumu akuti, mbuzi, moti anthu amaona ngati akunyoza mafumu. Mbuzi: Munthu wosamva. Chitsanzo: Iweyo ndiwe mbuzi, suumvayi. Mbuzitchire: Nyani. Mawu onena mwachining’a omwe ena amagwiritsa ntchito ponena za nyani. Amagwiritsa ntchito mawu amenewa akamafuna kumupanga ndiwo. Nanga aipe ndi dzina lomwe, bola kumupatsa lodyera. Chitsanzo: Lero aphika mbuzitchire. Mbwembwembwe: Zambirimbiri. Chitsanzo: (1) Nsalu mukufunazo zangati mbwembwemb- we. (2) Ngumbi zangoti mbwembwembwe. Mbwembwezera: Nyenyerera, kutaya pansi. Chitsanzo: Ndani amambwembwezera madeya apa? Mbwita: Kulephera kugwira kapena kupeza chinthu. Chitsanzo: (1) Amene wambwita adya mbewa yomwe wathawitsayo. (2) Anaponya bwino nkhwangwayo, koma wambwita. Mchikumbe: Munthu wolima kwambiri. Chitsanzo: Mchikumbe weniweni amayamba kulima akangomaliza kukolola. Mchimba (michimba): Manyi ouma. Chitsanzo: Agalu aunjika michimba kuseliko. Mchira wakhoswe: Chinthu chosachedwa kutha monga chuma. 248