Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 235
Paphata pa Chichewa
Makutu pekupeku: Munthu yemwe makutu ake
amangokhala m’mwamba kuti akamva nkhani
akaikhuthure kwina.
Chitsanzo: Kunyumba kwathu kunabwera munthu wa
makutu petupetu uja.
Makwacha: Ndalama zambiri.
Chitsanzo: Chaka chino ndipha makwacha.
Malamulo achitsulo: Malamulo okhwima.
Chitsanzo: Boma lakale lija linkakhazikitsa malamulo
achitsilo.
Malamulo okhwima: Malamulo ovuta kuwatsatira,
malamulo okhala ndi chilango chopweteka.
Chitsanzo: Anthu sakubanso chikhazikitsireni malamulo
okhwima.
Malango: Mwambo.
Chitsanzo: Mupite naye kumudzi akamupatse malango.
Malasankhuli: Mphalabungu, zinkhuwala.
Chitsanzo: Tinadyera malasankhuli.
Malata a pamutu: Dazi.
Chitsanzo: Ana a masiku ano sakumachedwa kukhoma
malata pamutu.
Malemu: Munthu womwalira.
Chitsanzo: Malemu amuna awo anawasiyira chuma.
Malipiro:
(a) Ndalama zomwe munthu amalandira akagwira ntchito.
Chitsanzo: Ntchito yonse imene ndikugwirayi, malipiro ake
angakhale amenewa!
(b) Zotsatira za zimene wachita. Nthawi zambiri mawuwa
amanenedwa ngati mkuluwiko munthu akakumana ndi
zotsatira za zochita zake zoipa.
Chitsanzo: Mimba watengayo ndi malipiro a uhule
amachita uja.
234