Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 230

Paphata pa Chichewa M’bandakucha: Mmawa kwambiri kusanache. Chitsanzo: Tinyamuka m’bandakucha. M’bedu: Chinagwa chokukuta. Chitsanzo: Mukandigulireko m’bedu. M’bindikiro (kubindikira): Kumangokhala m’nyumba kapena malo enaake osatuluka. Chitsanzo: (1) Anzanuwo ali pa m’bindikiro. (2) Mwanayu amangobindikira m’nyumba. M’bwaa: Nsapato. Chitsanzo: Ndagula m’bwaa inayake motchipa. M’kamwa mwa mbuzi: Zokwinyika. Mwina anthu amanena zimenezi chifukwa cha mmene mbuzi imatafuni- ra moti chinthu chimene chatuluka m’kamwa mwake sichingakhale chowongoka. Chitsanzo: Zovala zawo zikungokhala ngati zinali m’kam- wa mwa mbuzi. M’kamwam’kamwa: Aliyense kumangokamba zomwezo, nkhani imene yafala. Chitsanzo: Nkhani ili m’kamwam’kamwa ndi ya ukwati wawo. M’manja molakwika: Amanenedwa zinthu zikakhala kuti zapezeka kwa anthu osayenera. Chitsanzo: Zinthunzizi zikafika m’manja molakwika muk- azipezera patali. M’maso muli gwa! Mopanda manyazi. Chitsanzo: Amawatukwana mayi ake m’maso muli gwa! M’mbuyo mwa alendo: Kuchedwa, zinthu zitachitika kale. Chitsanzo: Pamene ankaganiza zoti anene chilungamo munali m’mbuyo mwa alendo. 229