Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 226

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Matenda aja angolowa libolonje moti tikukaiki- ra ngati atachire. (b) Kusokonekera, kuwonongeka, kuipiraipira, kufooka pa makhalidwe. Chitsanzo: (1) Sukulu yangolowa libolonje. (2) Dzikoli langolowa libolonje. Lowa m’chala: Kudwaladwala. Chitsanzo: Agogo masiku ano alowa m’chala. Lowa m’chikanamba: Chita manyazi. Chitsanzo: Anandichititsa manyazi kwambiri moti ndinangolowa m’chikanamba. Lowa m’chipiringu: Kulowa m’gulu. Chitsanzo: Anatizemba n’kulowa m’chipiringu ndipo sitinamuonenso. Lowa m’dzombe: Kulowa m’gulu. Chitsanzo: Wakubayo ataona kuti anthu ayamba kumuthamangitsa, anangolowa m’dzombe ndipo sanaonekenso. Lowa m’khutu (m’makutu): Sokosera. Chitsanzo: (1) Tamuuzani ali panjayo akhale chete aku- tilowa m’khutu (m’makutu). (2) Takhala chete ukutilowa m’khutu iwe! Lowa m’maso: Kusaona chinthu choti usankhe chifukwa zonse ndi zooneka bwino. Chitsanzo: Nsaluzi zandilowa m’maso, sindikuonapo yabwino yoti ndingasankhe. Lowa m’mimba (boola m’mimba): Kuvutitsa kwambiri, kuopsezedwa. Chitsanzo: Amanena zimenezi kuti angotiboola m’mimba. Lowa m’thengo: Kuchita misala. Chitsanzo: (1) Ukapitiriza kusuta chamba, ulowa m’then- go. (2) Achimwene awo analowa m’thengo. 225