Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 215

Paphata pa Chichewa Kuyenda: (a) Kucheza kapena kugwirizana kwambiri ndi munthu. Tanthauzo lenileni la mawuwa ndi kuchoka penapake kupita kwina pogwiritsa ntchito miyendo. Chitsanzo: Nanjekeya amayenda ndi Nasimango. (b) Kukhala pachibwenzi ndi munthu wina. Chitsanzo: Mtsikanayu amayenda ndi bambo awo! Kuyendana m’mapazi: Kulondanalondana. Chitsanzo: Sindikufuna zoyendana m’mapazi. Kuyendana pansi: Kokonzerana chiwembu kapena kukamba za anthu ena. Chitsanzo: Zoona osandiuza kuti mukupita? Apatu ndiye mwandiyenda pansi. Kuyerekedwa: Kuchita matama, kuvuta. Chitsanzo: Ambiri akalemera amayamba kuyerekedwa. Kuyeserera: Kuchita zinazake pongokonzekera. Chitsanzo: Ndisanasewere ndiyeserere kaye. Kuyezimira (kuyayamira): Kuchita dzanzi kwa mano. Chitsanzo: Ndikadya mango aawisi, mano anga amaye- zimira. Kuyezimira mano: Mano kuchita dzanzi. Chitsanzo: Ndinadya mango aawisi moti mano anga ayezimira. Kuyimba sukulu: Kuphunzira sukulu. Chitsanzo: Anyani anauza Sibo kuti akufuna kuimba nawo sukulu. Kuyoyoka thupi: Kuwonda. Chitsanzo: Atangowapeza nako anayamba kuyoyoka thupi. Kuyoyoka: (a) Kugwera pansi nthawi imodzi. Chitsanzo: Masamba ayoyokera pakhomo ponse. 214