Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 203

Paphata pa Chichewa Kutsinkha: Kudya ndiwo zokhazokha. Chitsanzo: Anawa akutsinkha ndiwo. Kutsira (kumwetsa): Kuchinya chigoli. Mawuwa amag- wiritsidwa ntchito pa masewera a mpira wa miyendo. Chitsanzo: Anyamata onse omwe anatsira (anamwetsa) zi- goli anawapatsa mendulo. Kutsitsa mpweya: Kuphwisa. Chitsanzo: Ndani wopanda nzeru amena watsitsa mpweya m’minibasi yopanda mawindo ngati ino! Kutsogoza: Kupha. Chitsanzo: Anakulakwirani chiyani kuti muwatsogoze asanadyerere? Kutsomphoka: (a) Kuchoka mwamphamvu. Chitsanzo: Lamba wa msamphawo anatsomphoka n’kumukwapula miyendo. (b) Kukula mofulumira. Chitsanzo: Mwanayu ndiye watsomphokatu, chaka chatha chomwechi anali wam’manja. Kutsuka m’kamwa: Kudya zakudya zankhuli. Chitsanzo: Tiphe nkhuku kuti titsukeko m’kamwa. Kutsukunyula: Kukalipira. Chitsanzo: Ngakhale mumutsukunyule sasintha. Kutsungula: Kulemera, kukhala ndi moyo wabwino. Chitsanzo: Anthu akusamuka m’mayiko osauka n’kumapita kumayiko otsungula. Kutsutsula pabala (pachilonda): (a) Kukumbutsa mavuto omwe munthu anakumana nawo. Chitsanzo: Zimene akuchitsazi akungotitsutsula pabala. (b) Kuputa munthu. Chitsanzo: Anthu amenewa akunditsutsula pabala. 202