Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 193
Paphata pa Chichewa
Kususuka: Kukhala wadyera.
Chitsanzo: Bambowa ndi osusuka.
Kuswa m’tu wangoma: Ulula zinthu zomwe
munapangana kuti simuulura. Ubongo wa ngoma
umakhala wowawa. Ndiye chimene chinachitika n’choti
munthu wina ndi mnzake anapita kwinakwake komwe
anamvako zachinsinsi ndipo anapangana kuti asaulule.
Koma atafika, winayo anayamba kuswa mutu wa ngoma.
Kuulula nkhani yowawa titero kunena kwake.
Chitsanzo: Tinagwirizana kuti tisanene chilichonse. Koma
titafika, anayamba kuswa m’tu wangoma.
Kuswa mphanje:
(a) Kuyamba kumene kuchita chinachake kapena kuyam-
bitsa.
Chitsanzo: Mukufuna kufunsira ndani? Tiuzeni tika-
kuswereni mphanje.
(b) Kuyamba kulima malo omwe sanalimidwepo.
Chitsanzo: Chaka chino ndikufuna kuswa mphanje.
Kuswa mtima: Kukhumudwitsa.
Chitsanzo: Nkhaniyi yaswa mtima wanga.
Kuswa mutu: Kuganiza kwambiri.
Chitsanzo: (1) Masamu amafunika anthu omwe amaswa
mutu kwambiri. (2) Nkhaniyi ndi yovuta zedi, yofunika
kuswa mutu.
Kuswa nthanga m’lichero: Ulula zinthu zomwe
munapangana kuti simuulura.
Chitsanzo: Tinagwirizana kuti tisanene chilichonse. Koma
titafika, anayamba kuswa nthanga m’lichero.
Kuswa: Kumenya.
Chitsanzo: Ukachitanso zimenezi ndikuswa.
Kuswaya: Kusiya kuwerengera munthu, kudana ndi
munthu.
Chitsanzo: (1) Atangolemera anawaswaya anzawo onse.
(2) Anatiswaya atangosamuka kuno.
192