Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 190

Paphata pa Chichewa (2) Mwana ameneyu amashupa kwabasi. Kushupika: Kuvutika kwambiri. Chitsanzo: Abale awo akushupika. Kusinira: Kugwiritsa ntchito zinthu mosamala, kudya pang’onopang’ono. Chitsanzo: Ndiwo ndakupatsanizi muzisinira. Kusinja mkonono: Kuliza mkonono kwambiri. Chitsanzo: Mwana uyu amausinja mkonono. Kusinja: (a) Kulira bwino. Chitsanzo: Wailesiyi ikusinja! (b) Kuphwanya zinthu. Chitsanzo: Sinjani chimangachi mumtondomo. (c) Kumenya munthu. Chitsanzo: Anzake amusinja koopsa. Kusintha maganizo: Kusiya zimene amaganiza n’kutsatira zina. Chitsanzo: N’chifukwa chiyani mwasintha maganizo achimwene? Kusisima: Mawuwa amatanthauza kulira mwapansipansi koma mopwetekedwa mtima. Koma angatanthauzenso zinthu zoola, ena amati zoonongeka. Chitsanzo: (1) Ndinawamva akusisima kuchipinda kwawo. (2) Ndiwo zijatu zasisima. Kusiya fumbi: Kuthawa. Chitsanzo: Ataona kuti zavuta, mnyamatayo anasiya fum- bi. Kusiya gaga: Kumwalira. Chitsanzo: Ukapitiriza khalidwe loipali usiya gaga. Kusiya m’gaiwa (gaga): Mawu achipomwe onena za mun- thu amene wamwalira. Chitsanzo: (1) Chigawenga chija chasiya m’gaiwa (gaga). (2) Ukapitiriza khalidwe loipali usiya m’gaiwa. 189