Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 185

Paphata pa Chichewa Kupyoza: (a) Kubaya. Chitsanzo: Nguluweyo anaipyoza ndi nthungo. (b) Kuwawa, kupweteka. Chitsanzo: Mawu amene anayankhula anandipyoza mumtima. Kusa: Kusonkhanitsa. Chitsanzo: Anakusa azimayi onse kuti akawapatse malangizo. Kusagwira kwa mutu: (a) Kusaganiza bwino, kusayenda bwino kwa mutu. Chitsanzo: (1) Koma mutu wako ukugwira? (b) Kusokonezeka, kusowa chochita. Chitsanzo: Mutu wake sukugwira. (c) Matenda a misala. Chitsanzo: Mutu wake sumagwira. Kusaimva: Kusalolera. Chitsanzo: Atamva zoti amamunyoza, nayenso sanaimve koma kumupitira komweko kuti akamutsire mphepo. Kusakhazikika: (a) Kumangoyendayenda. Chitsanzo: Musandidalile, ndine wosakhazikika. (b) Wopupuluma, obalalika. Chitsanzo: Mayiwa ndi wosakhazikika. Kusakwanitsidwa: Kusankhutira. Chitsanzo: Galuyu ndi wosakwanitsidwa, wamaliza zake akubweranso pano kuti amudyere nzakeyu. Kusala: (a) Kusadya kapena kusachitsa zinazake. Chitsanzo: Ine ndimasala zakudya zimenezi. (b) Kusakuwerengera, kukupatula. Chitsanzo: Anthuwa amandisala. 184