Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 158
Paphata pa Chichewa
Kulowerera:
(a) Kuyamba kuchita makhalidwe oipa.
Chitsanzo: Mwana uja analowerera.
(b) Kupitira kutsogolo, kupita kukakhala kutsogolo
n’kupitirira amene wawapeza.
Chitsanzo: Mwana uyu amakonda kulowerera.
Kuloweza: Kungozolowera kuti zimayenda chonchi.
Chitsanzo: (1) Akumangoyendera kuloweza. (2) Analoweza
kuti akabwera pano timamupatsa.
Kuloza chala: Kuimba mlandu.
Chitsanzo: (1) Ukasauka usaloze zala anzako omwe
zikuwayendera. (2) Zikawavuta amayamba kuloza chala
anthu ena.
Kululuzika: Kuchita manyazi.
Chitsanzo: Koma ndiye aluluzikatu! Akanadziwa sa-
kanabwera.
Kuluma khutu: Kuuza munthu nkhani yachinsinsi
pang’ono.
Chitsanzo: Upite kuti nawenso akakulume khutu.
Kuluma mwala: Kulephera, kukumana ndi mavuto.
Chitsanzo: Ukachita masewera uluma mwala.
Kuluma nauzira: Mawuwa anachokera ku zimene khoswe
amachita akamaluma chidendene kapena zala za munthu
n’kuuzira kuti asamve kupweteka kwambiri. Angatan-
thauze kupereka malangizo mwachikondi.
Chitsanzo: Bambo awa amaluma nauzira.
Kuluma pansi: Kugwa modetsa nkhawa.
157