Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 156

Paphata pa Chichewa Kulowa chamutu: Kubwera kapena kuchita nawo zinazake usanaitanidwe. Chitsanzo: Awa sanaitanidwe, angolowa chamutu. Kulowa chisawawa: Kuphweka, kumangochitidwa ndi ali- yense. Chitsanzo: (1) Ndinakana kusewera mpira chifukwa zinangolowa chisawawa. (2) Bizinezi ya mandasi yan- golowa chisawawa. Kulowa khutu ili n’kutulukira lina: Kusamva. Chitsanzo: Ukamuuza zinthu zimangolowa khutu ili n’ku- tulukira linalo. Kulowa kufa: Anthu ena amakhulupirira kuti bambo akamwalira pakhomo, pamafunika kuti munthu wina agone ndi mkazi wa munthuyo n’cholinga choti pakhomo- po pasachitikenso tsoka lina. Miyambo ngati imeneyi ndi imene ikukolezera moto kuti edzi ifale kwambiri. Chitsanzo: Malirowa akangoikidwa, mpofunika kuchita mwambo wa kulowa kufa. Kulowa limodzi ndi nkhuku: Kugona mwachangu. Chitsanzo: Anzanu aja amalowa limodzi ndi nkhuku. Kulowa m’chala: Kumangodwaladwala. Chitsanzo: Mayi awo alowa m’chala. Kulowa m’mabuku: Kufufuza zambiri m’mabuku, kuwerenga. Chitsanzo: Kuti tipeze yankho ya funso limeneli mpo- funika kulowa m’mabuku. Kulowa m’madzi: Kuwonongeka, kusaoneka phindu lake. Chitsanzo: Ndalama zanga zonse zangolowa m’madzi. 155