Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 150

Paphata pa Chichewa ndikaphe mpola. (2) Ndikufuna ndikwawire kumudzi kukaona matenda. Kukwawa: Kuyenda pang’onopang’ono. Chitsanzo: Chingolo chakechi chikungokwawa, tika- nakhala titafika tikanayenda wapansi. Kulabada: Kuwerengera, kulemekeza zomwe ena aku- nena. Chitsanzo: Salabada zoneneza za ena. Kulaka: Kukanika. Chitsanzo: Chalaka ameneyu palibe angachithe. Kulakatika: Kukambidwa. Tanthauzo lenileni la mawuwa amatanthauza kugwa pansi. Chitsanzo: Nkhani zimene zimalakatika zinali zokhudza kuipa kwawo. Kulala: Kutha, kuzilala. Chitsanzo: Moyo wathu ukulala ngati moto. Kulandirira m’matumba obooka: Kulandira ndalama n’kungopitirira. Chitsanzo: Ndalama timangolandirira m’matumba obooka. Kulanguluzika: Kuvutika. Chitsanzo: Amasangalala akamationa tikulanguluzika chonchi. Kulaulidwa: Kuyankhulidwa kapena kuona zinthu zo- chititsa manyazi. Chitsanzo: Sindinaonepo zimenezi pamoyo wanga, mwandilaula! Kulavula mwano: Kunena mawu achipongwe kapena am- wano. 149