Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 129

Paphata pa Chichewa (2) Mwana uyu ndi wogundika. (3) Ndinawapeza atagundi- ka ndi kuba ndiwo. Kugunyuza: (a) Kukumbutsa. Chitsanzo: Ndikakubwereka chinthuchi, ndisachite kudzakugunyuza kuti udzabweze. (b) Kugwedeza munthu kuti adzuke kapena akuyang’ane. Chitsanzo: Tawagunyuzani akugonawo. Kugupulira: Kulowerera nkhani ya eni. Chitsanzo: Mwanayu amangogupulira nkhani za eni. Kugwa chadodolido: Kugwa chagada, kugwa modetsa nkhawa. Chitsanzo: Anzanu aja anagwa chadodolido. Kugwa khunyu: Kudwala matenda akugwa. Chitsanzo: Mwanayu amagwa khunyu. Kugwa m’chikondi: Kuyamba kukonda munthu kapena chinthu china. Chitsanzo: (1) Mnyamatayu wagwa m’chikondi ndi mtsi- kana uja. (2) Ndagwa m’chikondi ndi filimu imeneyi. Kugwa m’dothi: Kukula, kutha msinkhu. Chitsanzo: (a) Ndinamufunsira asanagwe m’dothi. (b) Ana- siya sukulu atangogwa m’dothi. Kugwa m’papaya: Kusabereka. Chitsanzo: Amene ajatu anagwa m’papaya, moti ndi alonda chabe a akazi awo aja. Kugwa majini: Kugwidwa ndi mizimu. Chitsanzo: Pamaliro aja panali mayi wina yemwe anagwa majini. 128