Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 112

Paphata pa Chichewa Kudushula: Kuchotsa. Chitsanzo: Amudushula mutimu yawo. Kuduwa: Amenewa ndi mawu achipongwe omwe achinya- mata amagwiritsa ntchito ponena za munthu amene wamwalira. Chitsanzo: Akazi awo anaduwa. Kudwala m’mimba: Kuda nkhawa. Chitsanzo: Musatidwalitse m’mimba ndi nkhani zanu zon- gopekazo! Kudwala mwakayakaya: Kudwala kwambiri, kutsala pang’ono kufa. Chitsanzo: Achimwene awo akudwala mwakayakaya. Kudya buku: (a) Kuwerenga kwambiri. Chitsanzo: Kuti ukhoze mayeso umafunika kudya buku. (b) Kuphunzira kwambiri. Chitsanzo: Munthu ameneyu anadya buku. Kudya bwino: (a) Kulemera, kukhala ochita bwino. Chitsanzo: Banja ilo ndi lodya bwino. (b) Kudya zakudya zabwino. Chitsanzo: Ngakhale ali osauka koma amadya bwino. Kudya chipwete cha lunda: Kutenga nthenga kwa akazi kapena amuna. Chitsanzo: Ndinakumana naye akuyenda tang’atang’a. Zikuoneka kuti anadya chipwete cha lunda. Kudya kakaka: Kuseka. Chitsanzo: Ndinapeza aliyense akudya kakaka. 111