Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 100

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Achimwene, bwanji tipite paselipo tikabe khonde. Kuba tulo: Kugona. Nthawi zambiri amene amanena mawuwa amakhala amene akufuna kugona pa nthawi imene akugwira ntchito monga alonda. Chitsanzo: (1) Kodi munali kuti, mumaba tulo? (2) Ndili m’nyumbamu kaye, ndibe tulo. Kubabalika: Kupupuluma. Chitsanzo: Anzanuwa ndi obabalika. Kubadwa: Kuyamba. Chitsanzo: Dzina lakuti Nyasaland linabadwa pamene azungu anamva zolakwika kwa munthu wina yemwe ankalephera kumva chingerezi. Kubaizika: Kusaganiza bwino, misala. Chitsanzo: (1) Akukhala ngati wabaizika. (2) Munthu ameneyu ndi wobaizika. Kubaka: Kudya. Chitsanzo: Ndangomaliza kumene kubaka nsima. Kubaka: Kudya. Chitsanzo: Ndawaona akubaka nsima. Kubalalika: Kusokonezeka. Amatanthauzanso kumwa- zikana. Chitsanzo: Anzanuwa sachedwa kubalalika. Kubanda: (a) Kusokonekera mutu utasuta chamba. Chitsanzo: (1) Chamba chamubanda. (2) Akuoneka kuti wabandika. (b) Kukusangalatsa, kukumaliza. 99