Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 90

Miyambi ya Patsokwe Kudzinga ngati Mtiri, tionera Mende kutha. -Mtiri ndi mtundu wina wa mbewa ndipo mbewayi imakhala yofatsa. Kufatsa kumawombola. Osamapupuluma ngati mende wothawa moto, yemwe amaonedwa ndi osaka mbewa n’kuphedwa. Tizikhazikika kuti tione m’mene zithu zithere. Kudziwa kukoma kwa nyama n’kulinga utaidya. -Kuti munthu anene kuti chinthu ichi n’chabwino, amayenera kuyamba wakhala nacho. Kudziwa mphafa ya Buluzi n’kung’amba. -Ngati ukufuna kudziwa bwino nkhani inayake, umayenera kufunsa komanso kukhala wodekha. Kudziwana n’kutherana thumba lamchere. -Kuti udziwane ndi munthu umayenera kukhala naye kwa nthawi yaitali komanso kuchita naye zinthu zambiri. Kudziwika sikufanana ndi kukongola. -Si nthawi zonse pamene munthu angapeze mwayi chifukwa cha maonekedwe abwino koma makamaka chifukwa cha khalid- we labwino. Kudzudzulana kumamanga mudzi. -Kulankhulana momasuka kumathandiza kuti zinthu ziyende bwino pamalo. Kufa n’komwe, Tambala alira. -Ngakhale titamwalira sikuti tambala angasiye kulira. Mwam- biwu umatanthauza kuti tikalakwa, ngakhale tidzikometse kwa anthu, chilango chimakhalapobe. Komanso sikuti zinthu zin- gaime padzikoli ifeyo titamwalira. Kufula sundwe (khwimbi) ndi nzeru. -Sundwe ndi chakudya chakalekale. Kuti munthu atulutse chakudya chakele ndiye kuti anasunga penapake. Choncho, 89