Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 87

Miyambi ya Patsokwe Kuchenjera n’kosadya nako zabwino. -Munthu wochenjeretsa anzake amadzakhala pamavuto aakulu anzakewo akasiya kuchita naye zinthu. Kucheza sikudzala mtanga (dengu). -Kucheza kuyenera kukhala ndi malire n’cholinga choti tigwire ntchito. Kuchilendo, tema mbamu zofanana ndi eni nyumba. -Ukakhala kuchilendo umafunika kumachita zimene eni ake akuchita. Kuchiza nthenda n’kuyambiza. -Kuyambiza n’kuchita zinthu moyambirira. Kuti munthu athane ndi matenda, amafunika kuwatulukira akangoyamba kumene. Akakula amavuta kutuluka m’thupi. Komanso angathanthauze kuti, kuti mwana akhale ndi khalidwe labwino umayenera ku- mugwira dzanja n’kumamutsogolera, akalakwa osalephera ku- mupatsa chilango kuti awongoke. Kuchoka m’chiwaya n’kugwera pamoto. -Mawuwa amatanthauza kuchoka pa vuto lina n’kulowa m’mavuto ena aakulu kwambiri. Kuchoka muukonda n’kuleza. -Ukakhala pamavuto si bwino kumakokanso mavuto ena po- yamba kuyankhula zambirimbiri. Ndi bwino kumadekha kuti uchoke muukonde wa mavuto akupanikizawo. Kuchotsa mbola n’kuzula. -Kuti munthu achoke m’mavuto, ayenera kusiya chinthu kapena khalidwe limene lamuika m’mavutolo. Kuchulukana n’kwabwino, kumaipira kutha msuzi m’mbale. -Kuchulukana n’kwabwino, kumangoipira kuti zinthu siz- ichedwa kutha. Koma pakakhala ntchito imayenda ndithu. 86