Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 58

Miyambi ya Patsokwe Fodya amakoma ngwamnzako. -Mawuwa amatanthauza kuti chinthu chanzako n’chimene chimaoneka chokoma kuposa chako. Fodya m’panazale. -Ana amatengera zimene makolo awo amachita. Fodya n’kukhomo. -Munthu wina akapeza mnzake ali mnyumba mwake ndi mkazi wa mnyumbamo. Pomufunsa kuti “Ukutani m’nyumba mwan- gamo?” amati, “Ndikupempha fodya.” Mwini wakeyo amati: “Nanga kupempha fodya amachita kulowera m’nyumba.” Mwambiwu umatanthauza kuti tizichita zinthu modzilemekeza kuti tisasokoneza maganizo a anthu ena. Fodya wako ndi uyo ali pamphuno, wapachala ngwa mphepo. -Munthu ayenera kumakhutitsidwa ndi zomwe ali nazo, chifu- kwa zimene amafuna kapena amamva akhoza osadzazipeza pamoyo wake. Fodya wako ndi uyo ali pamphuno. -Tizidalira zinthu zomwe tili nazo kusiyana ndi zomwe tikungoganizira. Fulukutufulukutu kuti anzake kumudzi aziti akulima. -Sibwino kumangodzitama kapenanso kumachita zinthu modzionetsera. Ndi bwino kumagwira ntchito zooneka ndi maso m’malo momangodzitama. Ndi bwino kumachita zimene umanena. Fupa lokakamiza limagulula dzino. -Zinthu zokakamiza sizichedwa kutha ndipo nthawi zina zimao- nonga zinthu zina. 57