Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 53

Miyambi ya Patsokwe Dzenje la pida (pinji) limadziwika n’kuunjika. -Anthu akamapanda kukuyankhula kapena kumangokhala ndi msunamo umadziwa kuti pali nkhani. Dzera uko sikuyenda, koma tiye kuno. -Pophunzitsa ena ntchito kapena zinazake, si bwino kungofotok- oza chabe, tizionetsa chitsanzo chabwino kuti malangizo athu akhale aphindu. Dziko la eni ndi mowa, ukaponda waledzera. -Munthu ukayenda umayenera kukumbukira kuti ndiwe mlen- do. Ukalakwitsa zabwino zako zonse zimaiwalika. Dziko lingagwe. -Ukasiya ntchito yomwe munthu umagwira n’kuyamba ina ndiye munthu n’kumakufunsa: “Bwanji mutsirize kaye ntchito yomwe munayamba kaleyi?” Kuyankha kwake mokana umati: “Dziko lingagwe.” Dziko ndi mafuwa, achita kuchilikizana. -Munthu aliyense ali ndi mbali yake kuti zinthu ziyende bwino m’dziko kapena m’mudzi. Dziko ndi anthu, nyama ndi mambala. -Anthu ndi amene amakometsa dziko. Choncho, pafunika kuti anthu azigwirizana kuti zinthu ziziyenda bwino pamudzi pawo. Asamangokhala ngati nyama zomwe zimadyana zokhazokha. Dziko ndi mafuwa achita kuchinjiriza. -Kuti dziko liyende bwino pamafunika anthu ena oliteteza, ena odziwa zamalamulo ndiponso ena olamulira. Osangoti mfumu imodzi yokha ayi. Ngati zitakhala choncho mtendere sungakha- lepo. Dziko ndi wanu, ndalama ndi wathu. -Mawuwa amatanthauza kuti tinabwera kuno kudzapanga 52