Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 42

Miyambi ya Patsokwe ndi anthu basi. Choncho, tifunika kumawasamalira komanso ku- wapirira. Chingwe ndicho chithera msampha mphamvu. -Tikamangomvera nkhani zabodza za anthu ena tingadziputire mlandu. Zikhoza kutitsatira n’kupeza nazo mavuto. Chingwinjiri maliralira, chinalira m’msolo wa mbala. -Munthu ukakhala wapakamwa, umadzanena zinthu zina kwa ena omwe amafuna kudziwa zimenezo ndipo umapeza mavuto. Chinsanjesanje chinaoletsa mazira a mpheta. -Munthu wansanje amachedwa ndi kufufuza mkazi kapena mwamuna wake, potero amadziwitsa ena za khalidwe la mwamuna kapena mkazi wakeyo n’kudziwonongera banja. Chinsisi sichikhala pa anthu awiri. -Ukauza mnzako nkhani yachinsisi n’kumukhulupirira, uma- khala ukudzinamiza chifukwa nayenso amakhala ndi anzake ena apamtima. Chinthu chikataika chimalira mwini wake, monganso mwini wake ali kuchilira. -Ngati tatola chinthu chamwini tiyenera kuchibweza kuopera kuti chingatisowetse mtendere mumtima popeza timaoneka ngati tachiba. Chinthu ndi mtima, kanthu ndi khama. -Pamene waikapo mtima wako, uyenera kuchita khama kuti chinthucho chitheke. Chinziri chimanyang’wa ndi tsala lake (lakwawo). -Munthu aliyense amanyadira zinthu zake monga zovala, ntchi- to ndiponso banja lake. Chipande cha therere chimakoma n’kuyenderana. -Kuti mnzako akuchitire zabwino pafunika kumubwezera 41