Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 271

Miyambi ya Patsokwe Zipupa zili ndi makutu. -Tizionetsetsa tisananena zachinsinsi chifukwa makutu ali ponseponse. Zizikanika zitayang’anana. -Ndi bwino kumayesetsa kuchita khama pochita zinthu. Zichite kukanika zokha. Zizingokomera mbuzi kugunda galu, galu akati alumeko akuti waboola nguwo. -Munthu wokondedwa kapena wotchuka akachitira ena zoipa, si kawirikawiri kumudzudzula. Koma munthu wooneka ngati wopanda ntchito akachitira anthu ngati amenewa zoipa ama- landira chilango chokhwima. Zokoma zili m’tsogolo. -Munthu ukachita khama umadzakhala pabwino. Zolowere n’kudyere mwana. -Mawuwa amanenedwa pochenjeza munthu kuti akufuna aku- chitire zoipa pokunyengerera. Zonse ndi moyo. -Kuti munthu achite chilichonse amafunika kukhala ndi moyo. Munthu ngati ali moyo akhoza kuchita chilichonse chimene aku- funa. Zonse ndi nthawi. -Chilichonse chimachitika pa nthawi yake. Zumba likoma ndi nsinjiro. -Nkhani yongomva imapita iwonjerezeredwa mpaka imasokoneza zinthu. Zumba ndi masamba owawa. Amakonda ndi nsinjiro. 270