Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 269

Miyambi ya Patsokwe Zawombera mpeni. -Zomwe ndimafuna zalephereka, ndalephera. Zembeni kumowa, kumlandu andiitana. -Anthu ena amaitana anzawo zikavuta, zikamayenda amawa- taya. Zengerezu adalinda kwawukwawu. -Kuzengereza kumagwetsera munthu m’mavuto. Kungatileph- eretsenso kuchita zinthu zofunika kwambiri. Zidze pano n’za tonse. -Pamudzi pakagwa mavuto timayenera kuthandizana. Zigwinjiri maliralira, zinalira mumsongolo wa mbala. -Munthu wina ataba zingwinjiri anagwidwa zitalira m’thumba. Choipa sichingabisike chimaululika. Zika ukaona, Kamba anga mwala. -Kamba ngati sakusuntha amaoneka ngati mwala. Nkhani zina zimakhala zosamvetsetseka. Wina akhoza kudwala mwakayaka- ya, koma wina wolimba n’kumwalira kusiya wodwalayo. Zikachuluka sizidyeka. -Ndi bwino kumachita chinthu chimodzi pa nthawi imodzi. Zikagwera pamphuno sizidyeka. -Mawuwa amanena za munthu amene akulephera kugamula mlandu chifukwa choti ndi wa m’bale wake. Zikatalika zala ngati nkhonje wakhobwe. -Mawuwa amanena za munthu wakuba. Zikungokhala pachilowelo. -Mwambiwu umanena za anthu amene akubwera ku- madzapempha chifukwa choti amva zoti anzawo anapatsidwa. Mwachitsanzo, mwana akakhala m’chilowero anthu amabwera 268