Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 266

Miyambi ya Patsokwe Yagwa m’mbale ndi ndiwo. -Tisamasankhe ndiwo tikamadya. Yakondwa nkhwichi, Kalulu wakwiya. -Anthu ena sakondwa mnzawo akatukuka. Yangeyange adaphetsa kangaude. -Tiyenera kumachita zinthu mwadongosolo komanso mogwiri- zana kuti tisapeze mavuto. Yaphwa nyanja ana atole nkhombe. -Mauwa amanena za mavuto amene ana amakumana nawo chifukwa choti makolo awo amwalira. Yaponda thope yamwa. -Pakakhala chizindikiro chinachake ndiye kuti chinthucho chachitikadi. Yemwe umam’konda usamubwereke ndalama. -Munthu amene umamukonda akhoza kukukhumudwitsa ngati utamubwereka ndalama iyeyo osabweza. Posonyeza kumukon- da, popeza ambiri sabweza ngongole, ndi bwino usamubwereke. Yotema ndi nkhwangwa udzadya, ya mpeni sudzadya. -Munthu akatema nyama ndi nkhwangwa anthu ena amamva ndipo amabwera kuti adzadye nawo. Koma yodula ndi mpeni palibe amadziwa. Tisamachite zinthu modzionetsera. 265