Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 252

Miyambi ya Patsokwe Wakufa sadziwika. -Mawuwa amanenedwa anthu akamakangana n’kumanena kuti ndili ndi mphamvu kwambiri ndine. Nkhani yake imanena kuti, panali nkhanga ndi finye ndipo tsiku lina zonse zikuyenda zi- nakumana. Nkhanga inati: “Ndimakufuna iwe! Wafa lero! Koma finye anangoti: “Wakufa sadziwika!” Nkhanga inati, “Iwe ndi mwana wamwano eti? Ine ndikuti wafa lero!” Mmeneno n’kuti nkhanga itayamba kale kujompha finye, uku finye akutulutsa utomoni woyera womwe unali kukakamira pamlomo wa nkhan- gayo. Nkhanga inayamba kulephera kupuma ndipo inafa. Wogonja kapena wakufa sadziwika mpaka zonse zitafika pamapeto pake. Wakumba cha nje! mtengo wausiya. -Mawuwa amanenedwa ngati munthu walephera kupeza zimene amafuna kapena walephera kudziwa zoona zenizeni. Wakutsina khutu ndi mnansi. -Amene amakuchenjeza amakhala m’bale wako komanso ama- sonyeza kuti amakuganizira. Wakwatira kwa mphezi, saopa kung’anima. -Munthu amene akufunitsitsa chinthu ayenera kukhala wolimba mtima. Chilichonse chili ndi zovuta zake choncho si bwino kungosiya kuchita zinthuzo chifukwa choti ukukumana ndi mavuto. Ukamayamba kuchita zinthu umayenera kuganizira mavuto ake. Wakwatira mende, waleka chitute. -Mende samsunga chakudya anthu akangokolola, pomwe chi- tute amasunga. Ndiye munthu m’malo mokwara ndi mende wosunga chakudya, wakwatira mlesi weniweni chitute chifukwa cha kukongola. Tikamachita zinthu tizionetsetsa kuti tikusankha 251