Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 241

Miyambi ya Patsokwe Umachokera pamodzi ndi mawu. -Munthu akanena kanthu umayenera kuchita zomwezo osati zi- na. Umadikira kuti mafulufute atuluke. -Si bwino kumachita phuma pochita zinthu chifukwa zimenezo zingachititse kuti titaye mwayi kapena titsekezereze zabwino. Umaingitsa kachoka, walinga iwe nutola. -Munthu amene wakumana ndi zambiri ndi amene amayank- hula zogwira mtima. Munthu amene anali ndi khalidwe loipitsitsa ndi amene amaphunzitsa bwino. Umakongola ukusangalala, koma umabweza ukulira. -Ngongole imakoma ukamabwereka. Tizisamala ndi nkhani yobwereka ndalama. Umakumbukira mwana akapsa. -Kawirikawiri sitichenjeza anzathu mpaka atalowa m’mavuto. Umalawa zogagada ndi nkhwangwa, zocheka ndi mpeni suzi- lawa. -Tisamalakelake kukhala ndi zinthu zapamwamba kwambiri n’kumanyoza zing’onozing’ono. Umanena chatsitsa dzaye kuti Njovu ithyoke mnyanga. -Tizinena chayambitsa nkhani yeniyeni. Anthu ena ankadabwa kuti n’chiyani chathyola mnyanga wa Njovu. Atafufuza bwinob- wino anapeza kuti mumtengo wa maye munali nyani. Nyaniyo ndi amene anagwetsa dzaye kuti Njovu ithyoke mnyanga. Umanjata thumba tokoma tikuuluka. -Ena amabisa zoipa, koma akamamanga thumba lawo la zoipazo zina zimauluka n’kudziwika kwa aliyense. 240