Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 232

Miyambi ya Patsokwe Ukalemera, abale sakondwera. -Zinthu zikamakuyendera kapena ukakhala pabwino, anthu sasangalala. Amafuna kuti chinachake choipa chimuchitikire kuti mufanane. Ukalira mzinda usamapse mtima. -Ngati mfumu ikufuna kukhala ndi mudzi waukulu, iyenera kupewa kupsa mtima. Mtsogoleri amafunika kukhala woleza mtima. Ukamachoka umachoka bwino, suchoka utakhadzula mnzako mlomo. -Mlendo amayenera kuchoka bwino pamalo, apo ayi anthu san- gadzamulandirenso. Anthu sangalandire munthu amene wachoka pakhomo atakhadzula mlomo wa mnzake. Ukamafuna dzino lalitali, uzikhala ndi mlomo wovindikirira dzinolo. -Ukamawaputa mavuto kumadziwa kuti uthana nawo bwanji. Osamayamba kuchita chinthu ulibe mapulani. Ukanama sikuchedwa kucha. -Ukanena zabodza suchedwa kugwidwa. Chitsanzo: Ngati utanamiza wangongole kuti abwere mawa, sikumachidwa kucha. Ukaona chalero, usataye chakale. -Ndi bwino kumasunga zinthu zakale, osazitaya chifukwa choti tapeza zina. Ukaona mtanda kukula ndiye umati, “ndim’lere mwana wanuyu!” -Anthu ena amakonda kapena kuchitira zabwino anzawo akaona kuti apindulapo kenakake. Mwachitsanzo, kuuza mun- thu kuti amulelera mwana chonsecho akufuna amunyengerere 231