Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 22

Miyambi ya Patsokwe Chabadwa chafa, chili kumpani chauma. -Ngati munthu uli ndi moyo, dziwa kuti udzafa ndithu ndipon- so mavuto udzakumana nawo. Chadodometsa mleme chili ndi khambi. -Munthu akasiya chizolowezi chake ndiye kuti chilipo chimene chamudabwitsa kapena chamuchititsa mantha. Ukaona chomwe wina chamupezetsa tsoka, umayesetsa kupewa kuchita zomwe- zo. Chadza ndi yani chokwera ndi mwana kunkhokwe? -Tisamachite zomwe zingabweretsere ena mavuto. Kale anthu ankapewa kukwera ndi mwana munkhokwe kuopa kugwa ndi mwanayo n’kumuvulaza. Chadza ndi yani chopha nkhuku anzanu akudwala dzino? -Mawuwa amanenedwa munthu akachita zinazake zomwe akudziwiratu kuti nzake sachita nawo chifukwa akudwala kapena wapanikizika ndi zina. Chafa chaola, phwiti wasekera nthenga. -Munthu akamwalira, si anthu onse omwe amaliradi chifukwa cha chisoni. Ena amalira kwinaku akusangalala kuti adzatenge chuma chamasiye kapena adzalowe udindo wa womwalirayo. Chafuna mwini chili kwa Bongololo (kwa Mandala). -Munthu ukafunitsitsa chinthu, ndi bwino kulimbikira kugwira ntchito ndipo ukhoza kuchipeza. Chagwa pamtutu sichidyeka. -Mwambiwu umanena za munthu amene akulephera kugamula mlandu chifukwa mlanduwo ndi wa m’bale wake. Chagwera pamfuno sichidyeka. -Mwambiwu umanena za munthu amene akulephera kugamula mlandu chifukwa mlanduwo ndi wa m’bale wake. 21