Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 208

Miyambi ya Patsokwe Pamene pali ntchito pamakhalanso mavuto. Patsala paja pagona chinziri. -Nthawi zina ngakhale mlandu uweruzidwe, anthu amasungi- ranabe chakukhosi, enanso amadandaula kuti mlanduwo sunagamulidwe bwino. Amakhala ngati akunena kuti “patsala paja pagona chinziri.” Patse salira tololo. -Munthu wopemphetsa amafunika kungolandira zimene wap- atsidwazo. Mphatso simadzadza dengu. Patsogolo mpambuyo pomwe. -Nthawi zina amene ali patsogolo amatha kukhala pambuyo ngati anthuwo atauzidwa kuti atembunuke. Chimodzimodzi ndi mwayi umene ena ali nawo, mawa zikhoza kutembenuka n’kupezeka kuti ndi wathu. Paunjikana mtchembere pali bodza. -Azimayi akakhala pagulu nthawi zambiri amakonda kukamba mabodza. Paunjinji samabuulirapo. -Tisamayankhule pagulu zinthu zachinsinsi monga nkhani za m’banja ndi zina chifukwa zikhoza kungoyalutsa ife tomwe. Paunjinji savulirapo. -Nkhani zina zachinsinsi sitimaulula pagulu poopa kupusa. Paunyinji sabubulirapo. -Anthu ena omwe safuna kuti anzawo amveko zachinsinsi zawo amayesetsa kuti akambirane zachinsinsizo enawo akachokapo kapena amapita pamalo oduka mphepo. Pavinidwa mfulu, kapolo amavinidwa pomwepo. -Munthu amadyerera akakhala kuti amakhala bwino ndi anzake ochita bwino. 207