Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 206

Miyambi ya Patsokwe Pamudzi pakakhala pa zitsiru mkamwini asamakulirepo phazi. -Ukakhala pamudzi wa eni usamadzionetse kuti ndiwe wanzeru chifukwa sungadziwe zomwe eni mudzi amapangana. Pamudzi pamakoma ndi ana. -Pakhomo popanda ana sipasangalatsa. Pamudzi podziwadziwa, koma akusochera. -Mawuwa amanena za munthu amene akulephera kuchita chin- thu chimene akuchidziwa, ngati yemwe akusochera m’mudzi womwe wakulira. Pang’onopang’ono ndi mtolo. -Zinthu zikuluzikulu zimayamba ndi zinthu zing’onozing’ono. Mwambiwu umatiphunzitsanso kuti kuchita zinthu mwachifatse n’kothandiza kusiyana n’kuchita zinthu mopupu- luma. Panga chosankha utakwiya kuti kenako unong’oneze bondo. -Ukamachita zinthu kapena kumasankha zinthu utakwiya, umapezeka kuti wasankha kapena kuchita zinthu zolakwika n’kumadziimba mlandu pambuyo pake. Pankhondo sasekana. -Chibwana sichimafunika pantchito pa zinthu zofunika monga nkhondo. Pantchito mpachikamwini, amakuchotsa ndi usiku. -Ndi bwino kumakonzeratu zimene ungachite utachotsedwa ntchito chifukwa sudziwa kuti ndi liti pamene udzachoke. Ku- masamalira ntchito pogwira ntchitoyo molimbika. Pantchito n’kudyerana. -Anthu omwe amagwira ntchito limodzi amakonda kuchitira 205